Listen

Description

Tikaona pa vesi 15 ya 2 Timoteo chapter 3 Paulo akutiuza kuti Malemba Opatulika ali ndi kuthekela kutiunikila za chipulumutso kudzera mwa chikhulupiliro cha mwa Yesu Khristu. Ichi ndi chilungamo chochokela m’Baibulo chimene tikhazikikapo tsiku la lero. Baibulo ndi buku lodabwitsa limene lili ndi mphamvu zopulumutsa anthu osakhulupilira chifukwa choti Baibulo limalozela anthu kwa Yesu Khristu. Tikawelenganso Aheberi 4:12 tiona kuti Baibulo lili ndi moyo wodabwitsa.